Chewa
Surah Al-Kauther ( A River in Paradise) - Aya count 3
إِنَّآ أَعْطَيْنَٰكَ ٱلْكَوْثَرَ ﴿١﴾
Ndithu takupatsa zabwino zambiri (zina mwa izo ndi mtsinje wotchedwa Kauthar).[490]
فَصَلِّ لِرَبِّكَ وَٱنْحَرْ ﴿٢﴾
(Pakuti ndakupatsa zimenezo), pitiriza kupembedza Mbuye wako (moyera mtima) ndipo ipha nsembe yako (chifukwa chakuthokoza Allah pa zimene wakupatsa, monga ulemelero ndikukusankhira zabwino zambiri).[491]
إِنَّ شَانِئَكَ هُوَ ٱلْأَبْتَرُ ﴿٣﴾
Ndithu mdani wako ndiye ali wopanda mwawi. [492]